• Thu. Aug 3rd, 2023

Mtsogoleri wa Dziko lino a Lazarus McCarthy Chakwera afunira zabwino team ya mpira wamanja ya ma Queens

Aug 2, 2023

Tate wa fuko la Malawi Dr Lazarus McCarthy Chakwera wafunila zabwino team ya Malawi pamene ikusewera mpira wa mchembere mbaya mwa mnanu wa dziko lose lapansi ku South Africa.

Polankhula izi ku nyumba ya chifumu, a Chakwera ati ndipofunika kuti team ya ma Queens ipambane ma sewera ake chifukwa team imeneyi imatchuka ndi kuwina nthawi zonse.

A Chakwera poyankhura kudzera pa makina a internet anati iwo ndi boma lawo apitiliza kupempherera team imeneyi.

Ma Queens anayankha pamakina pomwepo kuthokoza mtsogoleriyu kamba kopeza nthawi yofunira zabwino atsikanawa omwe akhala akuchita bwino. Mwachitsanzo tikunena pano iwo agonjetsa kale ma Team a Scotland, Barbados ndi Fiji ku Cape Town komweko.

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

This site uses Akismet to reduce spam. Learn how your comment data is processed.